Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 82
Salimo la Asafu.
1 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
 
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
 
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
 
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
 
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

<- MASALIMO 81MASALIMO 83 ->