Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 67
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.
1 Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
 
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
 
6 Nthaka yabereka zokolola zake;
tidalitseni Mulungu wathu.
7 Mulungu atidalitse
kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

<- MASALIMO 66MASALIMO 68 ->