Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 30
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.
1 Ndidzakukwezani Yehova,
chifukwa mwanditulutsa kwakuya,
ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo
ndipo Inu munandichiritsa.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,
munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.
 
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;
tamandani dzina lake loyera.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi
koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;
utha kuchezera kulira usiku wonse,
koma chimwemwe chimabwera mmawa.
 
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,
“Sindidzagwedezekanso.”
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,
munachititsa phiri langa kuyima chilili;
koma pamene munabisa nkhope yanu,
ndinataya mtima.
 
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana;
kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga
ngati nditsikira ku dzenje?
Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?
Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;
Yehova mukhale thandizo langa.”
 
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;
munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.
Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

<- MASALIMO 29MASALIMO 31 ->