Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 16
Mikitamu ya Davide.
1 Ndisungeni Inu Mulungu,
pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
 
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;
popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,
amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina
mavuto awo adzachulukadi.
Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi
kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
 
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;
mwateteza kolimba gawo langa.
6 Malire a malo anga akhala pabwino;
ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
 
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;
ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.
Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,
sindidzagwedezeka.
 
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;
thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,
simudzalola kuti woyera wanu avunde.
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;
mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,
ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

<- MASALIMO 15MASALIMO 17 ->