Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 142
Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.
1 Ndikulirira Yehova mofuwula;
ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
2 Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
 
3 Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
anthu anditchera msampha mobisa.
4 Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
palibe amene amasamala za moyo wanga.
 
5 Ndilirira Inu Yehova;
ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
6 Mverani kulira kwanga
pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
7 Tulutseni mʼndende yanga
kuti nditamande dzina lanu.
 
Ndipo anthu olungama adzandizungulira
chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

<- MASALIMO 141MASALIMO 143 ->