Link to home pageLanguagesLink to all Bible versions on this site
Salimo 131
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.
1 Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,
maso anga siwonyada;
sinditengeteka mtima
ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa
ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,
moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
 
3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.

<- MASALIMO 130MASALIMO 132 ->