12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine, 13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena? 14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
Uthenga Wachinayi wa Balaamu
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati,
“Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori,
uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,
amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba,
amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse,
amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano;
ndikumupenya iye koma osati pafupi.
Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo;
ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli.
Iye adzagonjetsa Mowabu
ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
18 Edomu adzagonjetsedwa;
Seiri, mdani wake, adzawonongedwa
koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo
ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
Uthenga Wachisanu wa Balaamu
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: