4 Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5 “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6 Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 “ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8 Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 Ine ndinaganiza kuti
ndidzapita ku dziko la akufa
pamene moyo ukukoma.
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,
mʼdziko la anthu amoyo,
sindidzaonanso mtundu wa anthu
kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Nyumba yanga yasasuka
ndipo yachotsedwa.
Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,
ngati munthu wowomba nsalu;
kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;
koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,
ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,
ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.
Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.
Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 Koma ine ndinganene chiyani?
Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.
Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,
ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.