8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
<- 1 TIMOTEYO 11 TIMOTEYO 3 ->